It's about time to campaign!!
Are you ready to serve with me ,let us remember our God , nthawi ya Kampeni ikafika ,
Ine as your Shadow member of Parliament ndakonzeka kudzakutulutsani mumavuto ochuluka omwe inu a Malawi anzan ga mukukumana nanawo.
Just give me your Vote pa 16 September 2025.
Minandi-Akuka Likangala
Martha Minandi Akuka shado mp zomba Likangala people's party
Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Martha Minandi Akuka shado mp zomba Likangala people's party, Political Party, Blantyre.
08/10/2024
Ndife amodzi,palibe kusankhana kamba kosiyana mtundu, Zipembedzo komanso mu nkhani za Ndale.
Ichi ndi chimodzi mwa zomwe ndidzalimbikitse mu dera langa ndikalowa m'boma ngati phungu wa dera la Zomba Likangala mu chaka cha mmawa.
Yanyamuka
Mutu wankhani:
*Tonsefe ndi amodzi mu muzipembedzo ngakhalenso mu Ndale*
Ndinali ndi nthawi ina lero pomwe ndinalimbikitsa kuti mchitidwe wosankhana kamba kosiyana Zipembedzo uchepe mu dera langa .
Ndacheza ndi amayi a chipembedzo cha Chisilamu komanso ndinayendera anthu amipingo yosiyanasiyana kumpatikizapo mpingo wa katolika makamaka ndikuchita izi polingalira kuti mtsogoleri amayenera kuonetsa zitsanzo za bwino mu zonse pomwe akulangiza anthu ake m'dera lake.
Yanyamuka,
01/10/2024
Minandi Pledges Extra Support for Zomba Likangala Constituents - The Malawi Guardian People’s Party Shadow MP Martha Minandi (Akuka) has vowed to continue supporting youths affected by...
01/10/2024
I had time to visit some of the youths during a football Bonanza at Nambesa Village, Traditional Authority Mwambo in Zomba,where my constituency is, and here are some of the highlights
23/09/2024
Ndangoyambatu !!!!
Tiyeni tithamangile limodzi basi,
Zambiri zikubwera ,apa ndinali ndi nthawi ina yozisakaniza ndi achinyamata pomwe ndimakapereka mphatso ya mipira kwa atsikana ndi anyamata a m'dera langa pokonzekera Bonanza yomwe tikhale nayo posachedwapa.
Zangoyambatu weziwezi!!!
yanyamuka
20/09/2024
Polingalira kuti munthu wongopatsidwa kanthu tsiku ndi tsiku opanda pogwira penipeni sangatukuke pa moyo wake,ndinachezako ndi amayi ena m'dera langa ndikuwaunikira zina zomwe angamachite kuti adzipeza thandizo ndi kuthandizanso anthu ena monga odwala ndi ovutikitsitsa.
Mwa zina,ndapereka ndalama yokwana 100,000 Malawi Kwacha kwa amayi oposera 50 ,m'mudzi mwa Mack Moles, gulupu Nambesa mfumu ya ikulu Mwambo m'boma la Zomba kudzera mu gulu la amayi ena ukufuna kwabwino.
Ndawalimbikitsanso pa nkhani yochita malonda ang'onoang'ono kuti adzipeza mphindu la ndalama ndi kuyendera odwala m'zipatala ndi kuwapatsa zosowa zina monga soap komanso zakudya,mwa zochepa chabe.
Ndafikiranso anyamata ndi abambo ochita kabaza wa njinga za moto ndi kapalasa ndikuwathandiza powalimbikitsaso ndikangachepe kena.
Izi ndizomwe ndidzapitilize kuchitira anthu ndikadzalowa m'boma ngati phungu.
yanyamuka!!
26/08/2024
Pofuna kulimbikitsa anthu za kufunika kothandiza ena komanso kuika patsogolo ntchito za chitukuko m'madera, ndinayendera azimayi ena omwe anapanga magulu awo mu dera langa ndipo iwowo cholinga chawo ndikuchita ntchito za chifundo ndipo pa ntchitoyi ndathandizapo ndi thandizo la ndalama.
Ndinakwanitsanso kupeza mwayi okakhala nawo pa mwambo wazoperekapereka za m'mipingo sabata zingapo zapitazo.
Ndinapita Ku mpingo wina wa CCAP komanso wa Church of Christ m'dera langali komwe ndinapereka nawo kangachepe komwe ndinali nako.
Mukadzandisakha mu zisankho zikubwerazi chaka cha m'mawa, iyi idzakhala imodzi mwa ntchito zomwe ndidzapitilize mu ntchito zanga zina za chitukuko.
Izi ndi zina mwa zithunzi :
Click here to claim your Sponsored Listing.

10/04/2024
09/04/2024